07/03/2026
Phungu wa kunyumba ya malamulo mchigawo cha ku mmawa kwa kummwera kwa Blantyre walimbikitsa umodzi potukula derali.
Iye wati anthu akuyenera kugwira ntchito zosiyanasiyana zachitukuko mogwirizana posatengera kusiyana zokonda, kochokera, maonekedwe, udindo, ngakhalenso zipani.
Iyeyu wadzudzuranso anthu kuti achepetse kunyozana mmayankhulidwe, kufalitsa ma uthenga a bodza komanso kuipitsirana Mbiri koma mmalo mwake agwire ntchito yokomera zitukuko za mderali.
Pomwepo walimbikitsanso anthu amderali kutenga gawo pozindikira mavuto omwe alipo mderali ndikukaneneza kwa adindo oyenera.
Pa mapeto pake, walimbikitsanso adindo onse a mderali kuphatikizira oyang'anira chitukuko mmidzi komanso dera lonse kuti atenge gawo lalikulu potsogolera ntchito za chitukuko mderali.
Nkhaniyi yalembedwanso kuchokera pa zomwe, Ambiri Amatero analemba